The souls of hope

The souls of hope Souls of hope(SOHM) is a spiritual body that Ministers to the needy physical as well as spiritual choral spiritual gospel singers

09/06/2026

"pano pali chipiliro" nyimbo imodzi yopereka chiyembekezo..... title yake ndi Alinafe

okondedwa tikukuitanilani pa chochitika chomwe tikhale tikupanga unveil mwa Zina pa nyimbo zomwe zajambulidwa mu album imene ili mkudza
mwa Ina ndi imeneyi imene tikuti Mulungu Ali Nafe

zambiri zibwera koma tsiku ndi pa 27 June
iyiyi ndi music concert and fundraising tiyeni tikonzekere.

‎VISIBLE/LOCALIZED VS INVISIBLE CHURCH‎Lero tiyeni tioneko mitundu ya mipingo imene tilinayo pa dziko lapansi.‎‎okondedw...
04/06/2026

‎VISIBLE/LOCALIZED VS INVISIBLE CHURCH
‎Lero tiyeni tioneko mitundu ya mipingo imene tilinayo pa dziko lapansi.

‎okondedwa posatengera kusiyana zipembedzo kapena zikhulupiliro mipingo imagawidwa mmagulu awiri.localized komaso invisible church
‎kodi mipingo imeneyi ndi yosiyana bwanji??

‎LOCAL/VISIBLE CHURCH
‎localized church ndi mpingo umene Inu ndi Ine timapita kukasonkhana ndi anzathu,mpingo umenewu umatha kukhala pansi pa synod umatha kukhala pansi pa CMC umatha kukhala pansi pa ma diocese ndipo ma member a mpingo umenewu amakhala odziwika ndi kumatenga nawo mbari mu zochitika za ku mpingoko.
‎localized church imakhala ndi likulu imakhala ndi mfundo zoyendetsera mpingo ma church manual.localized church imalembetsedwa ku boma imakhala ndi Malo opemphelera atsogoleri sakwanitsa kudziwa mmene akhristu awo akuyendera Iwo chomwe amasunga ndi maina mu buku la mpingo komaso kutolera zachikhumi ndi zopereka Zina.
‎localized church AKA visible church imasungira anthu ochimwa komaso imasungira anthu abwinobwino kuli ngati kuchipatala ena amatelo.
‎localized church ndiyofunikira kwambiri chifukwa imakhala ndi azibusa amene amasamalira nkhosa komaso kuphunzitsa ziphunzitso za bible Madera akuti akuti.
‎chitsanzo Cha localized church ndi mpingo wa ku akolinto akolinto oyamba chapter one verse lachiwiri.

‎INVISIBLE CHURCH.
‎ku mmawa kuno okondedwa ndikukuitanirani mu church iyi yosaoneka ndi maso.imene bible likufotokoza za iyo pa 2 timoteyo 2:9 akuti Mulungu amawadziwa anthu ake
‎Okondedwa invisible church ndi gulu losankhidwa limene Iwo amene akumupembedza Iye mu Mzimu ndi mu choonadi Mulungu amawaika pawokha.

kusiyana kwa membership ya localized church ndi invisible church ndi kwakuti ku church kwathu komwe timapita timangowonana sitidziwa kuti awa dzulo apanga chani sitingawagwetse timakhala tilibe umboni pamene mu invisible church ma members ake amasanthulidwa mumtima aliyese payekhapayekha ndipo invisible church mulibe chinyengo.

‎uwu ndi mpingo umene Mulungu amati anthu anga,mpingo umenewu ulibe dera lopezekera ndipo amauwona ndi Mulungu Yekha.
‎Yobu anali mmodzi mwa anthu Opezeka Mu mpingo umenewu mpaka Mulungu adafika podziwa kuti Yobu sangakopeke ndi zilizonse.
‎onse amene amatsatira choonadi Cha Mulungu nasunga zonse zimene Mulungu adalamula Ali mu mpingo umenewu.
‎inde ma members a invisible church ndi ma members a localized church ndipo pamene nthawi ikufika kumapeto paoneka kusiyana kapena kugalukirana ma members a mu invisible church aoneka ogalukira komaso opanda uzimu.

‎ilipo mipingo imene imagalukira ndikumadziyerekezera kuti iyo ndi invisible church okondedwa mmawa uno invisible church simaoneka ndimaso ndi Mulungu Yekha amene amaona kuti awa Ali mu mpingo wanga awa ngakhale akuti Ali mu mpingo wa choonadi koma mu mpingo mwanga mulibe
‎mateyu 7:21,22



03/06/2026

Mulungu azilidalitsa banja ili.....................this day timkakonzekera kukalowa mu studio ndiye anatisamala ngati akwatitu

‎KODI TIKUYENERA KUGWADA NTHAWI ZONSE??‎fuso lomwe lidafusidwa linali limeneri‎yankho ndi AYI‎pali mapemphero ena safuni...
03/06/2026

‎KODI TIKUYENERA KUGWADA NTHAWI ZONSE??
‎fuso lomwe lidafusidwa linali limeneri
‎yankho ndi AYI
‎pali mapemphero ena safunikira kuti ugwade.
‎driver angathe KUPEMPHERA mumtima Ali mkati moyendetsa galimoto
‎Hezekia adapemphera Ali pa bed pake Ali mkati modwala
‎pali zinthu Zina za dzidzidzi zimene sumayembekezera kuti ungathe kukumana nazo ungathe kumuwuza Mulungu kuti ambuye takhala naneni mu nthawi iyi.
‎tisaiwale kuti pemphero ndiko kumuwuza Mulungu nkhawa zathu,kumuthokoza komaso kumupempha kumene.
‎niye fuso ndikumati nanga kugwada kuli ndi phindu lanji??
‎monga mmene kuli kutseka maso kugwada pamaso pa Mulungu kumaonetsera zinthu zingapo.

‎olemba wina adalembako mu buku Lina lotchedwa selected messages book 2 tsamba 312 adalemba kuti kugwada tikamapemphera kumaonetsa kuti tikumudalira Mulungu kwa thunthu ndipo mkoyenera kugwada tikamapemphera.

‎mu selected message book 3 tsamba 266 akupitiliza kufotokoza kuti ngakhale kugwada kuli koyenera koma Mulungu amamva mapemphero athu ngakhale amene sitidagwade.
‎mu buku Lina lotchedwa kuti mapazi opita kwa Yesu tsamba 99 olemba yemweyu akufotokoza kuti tingathe KUPEMPHERA Malo ena aliwonse ngakhale mu chipwiilikiti Mulungu amamva pemphero ndithu.

‎Nanga bible likuti chani nkhani ya kugwada kapena kusagwada
‎masalimo 50:15 akuti ndiyitaneni pamene zakuvutani ndipo ine ndidzakupulumutsani
‎David mmene amkamenyana ndi Goliyati sanagwade pansi ndikupemphera koma Mulungu adamuthandizira

‎WORSHIP VS PRAYER
‎ idzani nonse timpembedze ndikumugwadira Bondo lililonse limugwadire amene adatilenga masalimo 95:6
‎pali kusiyana pakati pa KUPEMBEDZA komaso KUPEMPHERA
‎kupemphera tanena kale kuti ndi kupereka uthenga kwa Mulungu nthawi iliyonse pamene KUPEMBEDZA ndi kuonetsera kapena kuchita zinthu zimene zipereke Ulemu kwa Mulunguyo
‎mwachitsanzo pa ora lopembedza tikuyenera kugwada pamaso pa Mulungu
‎pa ora lopembedza tikuyenera kupereka chuma chathu kwa Mulungu
‎pa ora lopembedza tikuyenera kusiya zinthu zathu zonse ndi kupanga concentrate za Mulunguyo.
‎ndichifukwa chake pemphero la pa devine tonse timafusidwa kugwada chifukwa nthawi imene ija ndi ora lopembedza

‎PEMPHERO ‎mau akuti pemphero safikira penipeni pa tanthauzo lake chifukwa pemphero silitanthauza kupempha kokha koma li...
02/06/2026

‎PEMPHERO
‎mau akuti pemphero safikira penipeni pa tanthauzo lake chifukwa pemphero silitanthauza kupempha kokha koma limatanthauza kupereka nkhawa,mathokozo,kapena uthenga uliwonse kwa Mulungu.
‎kawirikawiri tikapemphera timakhulupilira kuti Tayankhidwa koma nthawi Zina timakhala kuti sitinayankhidwe,penaso pemphero silinafike.

‎ena ochepa mwa ma verse amene akukamba za pemphero
‎1 thessalonians 5:16-18,Mathews 21:22, Philippians 4:6

‎kodi pemphero ndi la mphamvu bwanji?? ndi paja pamabwera maumboni paja...komaso ndipaja timalowa mu bible kukawona anthu amene adapemphera ambiri mbiri
‎koma fuso lofunikira kwambiri ndi lakuti kodi KUPEMPHERA kuli ndi nthawi
‎zimenezi zingathe kuyamba kutipatsanso chithunzithunzi kuti kodi ngati kulibe nthawi nanga kuliso ndi kakhalidwe kake??
‎okondedwa pa 1 thessalonians 5:17 akunena kuti tizipemphera kosalekeza kusonyeza kuti KUPEMPHERA si mu church Mokha nthawi zonse tikuyenera kukhala tapemphera.
‎anzathu a chi slam amayenera KUPEMPHERA 50 times a day koma chifukwa chofuna kupereka mpata ku zintchito adachepetsa amapemphera 5 times a day
‎okondedwa satana amakhala akuyesera every second kuti munthu akhale ochimwa ndithu opanda pemphero palibe chomwe chingayende
‎pemphero limateteza,pemphero limasintha nyengo,pemphero limachiza nthenda pemphero limafewetsa mitima ya Adani ndipo pemphero limasokoneza ma plan a kumidima.
‎kodi pemphero likuyenera kuchoka pakamwa pokha??
‎yankho ndi ayi ,pemphero likuyenera kuchokera mumtima
‎kusiyana kwa Mulungu ndi mabwana athu a ku office ndikwakuti mabwana athu a mzintchito amafuna amve mau kapena tiwalembere kalata koma Mulungu wathu amawerenga maganizo athu
‎pamene taganiza zofuna kumchitira wina zabwino Mulungu amakhala wadziwa kale ndipo pamene tikumupempha mu malingaliro athu Mulungu amakhala akumva.
‎mwapempherako Inu mu minbus pamene driver akuthamangitsa kwambiri.
‎Mumati Ambuye chonde tithandizeni kuti galimotoyi isachite ngozi
‎Hannah akuti samkatulutsa mau pakamwa pake pamkangogwedera ndipo Eli adafika pomuganizira kuti waledzera
‎koma mu mtima mwa Hannah mudali mapemphero 1 Sam 1:26

‎CONCLUSION
‎1.kupemphera ndi nthawi Ina iliyonse
‎2.Mulungu amamva pemphero ngakhale osatulutsa Mau
‎3.kupemphera si kupempha zosowa kokha komaso kuyamika,ngakhaleso kupembedza
‎4.mu pemphero muli mphamvu

30/05/2026
30/05/2026

Happy Sabbath okondedwa
mukubwera kudzapemphera pa Salima Central SDA Church kodi?? tidziwitseni

nanga lero mupemphera ku??
kapena simupemphera lero tidziwe nawo komwe mumapemphera

akuimbawa ndi a The souls of hope mutu wa nyimbo ndi

‎FROM INBOX‎talandila mafuso awiri kuchoka ku inbox fuso loyamba akufuna kudziwa kuti kodi nkhani yopemphera ndikoyenera...
28/05/2026

‎FROM INBOX
‎talandila mafuso awiri kuchoka ku inbox fuso loyamba akufuna kudziwa kuti kodi nkhani yopemphera ndikoyenera kumagwada nthawi zonse pamene tikupemphera ? mukukamba kwawo akuti adakumanako ndi chiphunzitso chokamba zogwadwa nthawi zonse ndipo ngati simudagwade pemphero limenero kumwamba silidamveke.

‎tikhala ndi ma presentation angapo
‎presentation yoyamba tione kuti kodi akati pemphero ndi chani nanga kodi Mulungu amatha kumva pemphero la mumtima??kusiyana kwa KUPEMPHERA ndi ku LAMBIRA

‎presentation yachiwiri ikhala ya anthu amene adapemphera ndipo tiona kuti kodi onsewa adagwada? komaso tidzaona kuti nchifukwa chiyani timagwada??

‎pomaliza presentation tidzaona kuti kodi Mulungu amayankha pemphero liti?? nanga kodi kutsinzina kuli ndi phindu lanji??

‎koma padakali pano okondedwa titha kuika maganizo athu mmene timamvera nkhani ya pemhero kodi ndikoyenera kumagwada pa pemphero lililonse??

‎note . zithunzi ndizopanga generate ndi AI

‎ZIGAWO NDI UKULU MU MPINGO WA SEVENTH-DAY ADVENTIST CHURCH.‎Mpingo wa seventh day uli ndi mmaudindo komaso zigawo kuyam...
26/05/2026

‎ZIGAWO NDI UKULU MU MPINGO WA SEVENTH-DAY ADVENTIST CHURCH.
‎Mpingo wa seventh day uli ndi mmaudindo komaso zigawo kuyambira ku mwamba kutsika pansi Lero tiyeni tione zomwe church manual akutifotokozera zokhudza maudindo komaso zigawo.

‎GENERAL CONFERENCE.
‎mukadzamva za general conference kumeneku ndiye ku headquarters kumene kumapezeka wamkulu komaso akulu akulu otsogolera mpingowu.
‎kumeneku ndikomwe kumapangidwa mfundo zoyendetsera mpingo pa dziko lonse lapansi.ku general conference ndi komwe kumathera milandu yonse imene yakanika kukambidwa mu mpingo ndipo president amakhala ndi mphamvu zopanga chiganizo pa nkhani zomwe zakanika kukonza kumusi.

‎DIVISION
‎mukadzamva za Division osadzabalalika iyi ndi general conference yomweyi koma apapa amakhala kuti ayigawa malingana ndi zigawo/maiko oyandikana.mwachitsanzo if kwathu kuno tili mu SID kapena kuti maiko amene Ali kummwera kwa nyanja ya India mtsogoleri wathu wambari ya kunoko ndi member wa general conference.izizi zikutanthauza kuti General conference ntchito yake imagwilira mu ma division ndipo adindo amene amakhala ku general conference amalandila ma report kuchokera mu ma division president aliyese wa ku division amakhala wachiwiri wa president wa ku general conference Mwachidule general conference simakhala ndi vice president mmodzi.

‎UNION CONFERENCE
‎union conference ndi chigawo chimene chimalinganizidwa ndi general conference/Division nthawi zambiri limakhala dziko lonse or ngati anthu ake Ali odzidalira mu dziko mumatha kukhala ma union conference awiri nthawi Zina chifukwa Cha kukula kwa dzikolo.
‎union conference imakhala ndi mphamvu yodzisankhila atsogoleri komaso imadzisamalira yokha pa nkhani za chuma.

‎UNION MISSION/FIELD
‎union mission ndi ng'ono wake wa union conference ichi ndi chigawo cholinganizodwa ndi general conference koma chosaima pachokha.awawa amadalira ku division ku nkhani za chuma komaso odzasankha atsogoleri amachita kuchoka ku division

‎CONFERENCE
‎Union conference/field imathaso kugawidwa mu kachigawo kena kamene kamatchedwa kuti conference aka ndi kachigawo kamene kamakhala kuti kakula mu chuma,ndipo kamakhala ndi ulamuliro paokha odzisankhira adindo komaso amakhala ndi ma structure awo okhazikika.

‎FIELD/MISSION
‎Aka ndi kachigawo kamene kamagawidwa kuchoka mu union conference/mission koma kamakhala kosaima pakokha awawa samasankha maudindo paokha koma ku union kumachoka akuluakulu kudzathandizira komaso amadalira ku union mu zinthu zambiri.

‎DISTRICT
‎ma conference/field amagawidwaso mu ma district.awa amakhala Madera amene ayenerezedwa kuti angathe kukwanitsa kusamalira abusa komaso kumbari ya zachuma akuchita bwino.abusa amapita kukakhala pa centre mu district mumakhala ma church olinganizidwa atatu kapena kuposera apo amene amagawana ma resources


‎ZONE
‎ma district amene akukhala moyandikizana amathaso kumagawana ma resources akakumana ma district amenewa amatchedwa kuti zone.

Address

Salima Central Along Side Takomana Road
Salima

Telephone

+265884943622

Website

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when The souls of hope posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Organization

Send a message to The souls of hope:

Share