Friends of Katema,Mangochi

Friends of Katema,Mangochi BRINGING THE PEOPLE OF KATEMA,MANGOCHI MALAWI TOGETHER

 Apolisi m'boma la Mangochi amanga abambo atatu ndi mai mmodzi powaganizira kuti apezeka ndi matumba a makala 108 popand...
09/05/2026



Apolisi m'boma la Mangochi amanga abambo atatu ndi mai mmodzi powaganizira kuti apezeka ndi matumba a makala 108 popanda kalata zowavomereza.

Ofalitsankhani za polisi ya Mangochi, a Amina Tepani Daudi, ati oganiziridwawo ndi a Hawa Kambwiri, Austin Sharifu, Harry Haj, komanso a Shaibu Jonas.

“Anthuwa agwidwa usiku wapa 8 May, 2026 ku Bolera munsewu opita ku Chilipa,” a Daudi anatero.

Anthuwa akaonekera kubwalo lamilandu kukayankha mlandu opezeka ndi makala popanda chilorezo.

Wolemba: Davie Umar

Lero Taludza Harrison Allie, Kwa Msosa amene ndi mwana wa M'bulindi ku Mtalala. Anali Mnyamata waluso loyomba nyimbo. Mz...
04/05/2026

Lero Taludza Harrison Allie, Kwa Msosa amene ndi mwana wa M'bulindi ku Mtalala. Anali Mnyamata waluso loyomba nyimbo. Mzimu wake uwutse mu Mtendere.

02/05/2026

Akutero kuche Mawiriga

28/04/2026



Anthu omwe akuwaganizira kuti amachita malonda owotcha makala, dzulo akuti alanda mfuti ndi zipolopolo kwa apolisi awiri aku Chilipa m'boma la Mangochi.

‎Akulu akulu akumidzi oteteza nkhalango ku Chilipa awuza Times kuti iwo anatengana ndi apolisiwo ndikulondola galimoto lina lomwe akuti linanyamula makala ochokela munkhalango yotetezedwa ya Phirilongwe m'bomali.

‎Izi zinachititsa kuti apolisiwa atchingire galimotoli pansewu.
Koma iwo ati galimotili linakwanitsa kuthawa, ndipo apolisi awiriwo anathamangira galimotolo pa njinga ya moto koma atalipeza, mavendawa popeza anali ambiri anakwanitsa kulanda mfuti ya K.2.C ndi zipolopolo zake zonse.

‎Mneneri wa polisi ya Mangochi, a Amina Daudi watsikimiza za nkhaniyi ndipo wati pakadali pano, Apolisi ochokela pa Boma apita kale kuchilipa kukafufuza za nkhaniyi.

Wolemba Yohane Symon

‎ ‎‎Mfuti ya mtundu wa K2C yomwe anthu omwe akuwaganizira kuti ndi mavenda a makala analanda apolisi a pa Chilipa m'boma...
28/04/2026



‎Mfuti ya mtundu wa K2C yomwe anthu omwe akuwaganizira kuti ndi mavenda a makala analanda apolisi a pa Chilipa m'boma la Mangochi dzulo, tsopano yapezeka.

‎Mneneri wa polisi ya Mangochi, a Amina Tepani Daudi, wati gulu la apolisi lomwe kum'mawaku motsogozedwa ndi Senior Suprentendent Gideon Chisale, linathamangira kumeneko ndi lomwe lapeza mfutiyo, yomwe ati anthuwo anayitaya kufupi ndi dziwe lotchedwa Kateza.

‎Komabe, a Tepani Daudi ati apolisi apeza zipolopolo zisanu zokha mwa zipolopolo khumi zomwe anthuwo analanda, ndipo ntchito yosaka zipolopolo zisanu zotsalazo ili mkati.

‎Muli phwando lotentha makala, kucheka matabwa ndi nkhuni m'nkhalango ya Phirilongwe m'boma la Mangochi, momwe ena anamanga maziko momwemo, koma kulibe chitetezo choletsa izi kuchitika kapena kupitirira.


‎(by Western Guta-Mangochi:04/28/2026)

Anthu osadziwika omwe akuganizilidwa kuti ndi akuba akhapa Gogo wina wamkazi mpaka kupha mmudzi wa Mwawa usiku wa pa 24/...
25/04/2026

Anthu osadziwika omwe akuganizilidwa kuti ndi akuba akhapa Gogo wina wamkazi mpaka kupha mmudzi wa Mwawa usiku wa pa 24/4/25. Anthuwa akuganizilidwa kuti aba Chimanga koma sakudziwika omwe apanga chipongwechi.

Pakadali pano a police kuchokera ku Mangochi afika kumalo ku.

Mzimu Wa gogo athu uwutse mu mtendere

18/03/2026

Big shout out to my newest top fans! Leno TG, Hope Zatha, Laika M Mude, Mgk Frazer, Tholo Adam, Dáń-b Bùlèýá, Meleka Msosa

10/02/2026



Ofesi ya zaumoyo m'boma la Mangochi yatumiza akatswiri a zaumoyo ku dera la Katema, kuti akafufuze zomwe akuti ndi nthenda ya chilendo, yomwe yabuka kumeneko ndipo yakhudza kale anthu 56.

Mneneri wa ofesiyi, a Harold Kabuluzi, wati ofesi yawo yatumiza akatswiriwa kamba ka kuchuluka kwa malipotiwa, omwe akatswiriwa ndiwo adzafotokoze zoona zenizeni zomwe akapeze.

M'modzi mwa anthu a m'derali, a Mussah Ibrahim, wauza Zodiak Online kuti kuyambira pafupifupi sabata zitatu zapitazo, anthu akumamva mutu waching'alang'ala, kupweteka ndi kutsekula m'mimba komanso kusanza.

A Ibrahim ati izi ndi zodabwitsa kuti anthu ochuluka chomwechi adwale zofanana m'mudzi umodzi, ndipo ngakhale palibe wamwalira, akupempha adindo pa zaumoyo kuti achite machawi kufufuza.

Iwo ati padakali pano, anthu ena akumwa zomera ngati mankhwala, ati kamba kakuti mankhwala akuchipatala sakuthandiza. Apa iwo ati enanso mwa odwala sakupita kuchipatala chifukwa chakutalikira kwa madera awo.

(by Western Guta-Mangochi:02/10/2026)

 Polisi ya Mangochi yati ndi yokonzeka kutsegulanso polisi yaying'ono ya kwa Katema m'dera la Mfumu Mponda ngati anthu a...
13/01/2026



Polisi ya Mangochi yati ndi yokonzeka kutsegulanso polisi yaying'ono ya kwa Katema m'dera la Mfumu Mponda ngati anthu a derali atakonza zonse zomwe adaononga pa malo pomwe panali polisiyi.

Anthu a derali, mu mwezi wa March chaka chatha, atasemphana ndi apolisi adaphwanya polisiyi kuphatikizapo nyumba za achitetezo, katundu wawo ngakhalenso kuotcha katundu wa mu ofesi monga mipando ndi zina.

Izi zinapangitsa mkulu wa polisi m'bomali kutseka malowa, zomwe panopa zabweretsa mavuto ochuluka akusowa kwa chitetezo monga umbava woba ziweto, mbewu za ku munda, ndi zina zambiri.

Malingana ndi a mfumu a Mponda-Mponda akuti panopa zinthu sizili bwino ndipo apempha apolisi kuti awathandize pobweretsanso apolisi ku derali.

"Tikugwada pa maso pawo kuti tachimina ndipo sitidzachitanso. Tazindikira kuti polisi ndiyofunikira," anatero a mfumuwa.

Koma m'mawu ake mneneri wa polisi ya Mangochi Amina Tepani Daudi wati iwo ndikonzeka kutumiza anthu awo achitetezo koma pokhapokha anthu a derali atakonza ofesi yomwe anaphwanya komanso nyumba za anthu achitetezowa.

(Wolemba: Ayamba Kandodo—Correspondent)

Let's follow WhatsApp Channel via this 👇 link(friends of Katema Mangochi) https://whatsapp.com/channel/0029Vb7G818JENy8p...
12/01/2026

Let's follow WhatsApp Channel via this 👇 link
(friends of Katema Mangochi) https://whatsapp.com/channel/0029Vb7G818JENy8pEEETM2P

Follow Friends Of Katema, Mangochi's WhatsApp channel. Promotion of unity among Katema People.. Join 1 follower for the latest updates.

Address

Chilembwe Road
Mangochi

Website

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Friends of Katema,Mangochi posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Share