Mudzi wathu news online : Nkhani Zenizeni, zodalirika

Mudzi wathu news online : Nkhani Zenizeni, zodalirika Contact information, map and directions, contact form, opening hours, services, ratings, photos, videos and announcements from Mudzi wathu news online : Nkhani Zenizeni, zodalirika, Youth Organization, Msanje Mpaka Chitipa, Lilongwe.

πŸ‡²πŸ‡Ό ONJEZANI KENANI ATSUTSIDWA KU FUNDO YAKE YOKHALA KUMBALI YA MEC PODELERA BOMAKusanthula kwa Symon Mandawala yemwe ali...
31/05/2026

πŸ‡²πŸ‡Ό ONJEZANI KENANI ATSUTSIDWA KU FUNDO YAKE YOKHALA KUMBALI YA MEC PODELERA BOMA

Kusanthula kwa Symon Mandawala yemwe ali ku United States of America wabweletsa umboni wochuluka wosonyeza kuti Malawi Electoral Commission ikhoza kusamutsidwa ndi boma kupita kumalo ena aliwonse ku Malawi.

Umboni woyamba wochokera ku United States of America. Trump adapambana milandu yonse yomwe inkafuna kuti mabungwe ngati Trade Commission ndi Labor Relations Commission akhale odziimira pa boma. Khoti lalikulu kwambiri ku United States of America linanena momveka bwino kuti ngakhale bungwe ligwire ntchito mwa ufulu wake, silingathe kudzidula pa ulamuliro wa boma. Milandu imeneyi inagwiranso mabungwe akunja ngati USAID.

Umboni wachiwiri ndi wa m'lamulo la Malawi. Gawo la m'lamulo limapatsa Malawi Electoral Commission mphamvu zochita ntchito za zisankho popanda kulamulidwa ndi boma kapena pulezidenti. Koma gawo lomweli limaperekanso kuti ndalama zonse za bungwe zizichokera ku bajeti ya boma. Izi zikutanthauza kuti boma lili ndi dzanja pa moyo wa bungwe kudzera mu ndalama.

Umboni wachitatu wochokera ku mayiko ena. Ku South Africa Independent Electoral Commission imagwira ntchito mwa ufulu wake koma imadalira ndalama za boma la South Africa. Ku Kenya ndi Uganda nkomweko. Mayiko ambiri ku Africa mabungwe a zisankho amadalira ndalama za boma. Izi zikusonyeza kuti ufulu wa ntchito ndi wosiyana ndi ufulu wazachuma.

Umboni wachinayi ndi wakuti ngati Nyumba ya Malamulo ingapange lamulo latsopano lochotsa boma pa udindo wopereka ndalama ku Malawi Electoral Commission, pamenepo bungwe lidzakhala lodziimira kwathunthu. Koma mpaka pano lamulo loterolo palibe.

Malingana ndi kusathura, Mandawala wamaliza kunena kuti ntchito ya Malawi Electoral Commission ndi yodziimira. Koma pazachuma silodziimira pa boma. Chifukwa chake boma likhoza kuisamutsa kumalo kulikonse mkati mwa Malawi osasintha ntchito zake za m'lamulo.

MUDZI WATHU NEWS ONLINE πŸ“° | NKHANI ZENIZENI, ZODALIRIKA .

Olemekezeka Dr. Shadric Namalomba ati ufumu samalowa munthu wakunjira amalowa ndi mwana wapa nkhomo iwo ayakhula izi pa ...
31/05/2026

Olemekezeka Dr. Shadric Namalomba ati ufumu samalowa munthu wakunjira amalowa ndi mwana wapa nkhomo iwo ayakhula izi pa michongwe ground.

Iwo amema anthu kuti asakhe mwana wa chipani Cha Democratic Progressive Party Francis Haiya ngati MP wa Mikoko constituency pa 30 June pa masankho achibwereza.

MUDZI WATHU NEWS ONLINE πŸ“° | NKHANI ZENIZENI ZODALIRIKA.

πŸ‡²πŸ‡Ό  PHWETEKEERE AKUCHOKERA KU SOUTH AMERICAPhwetekere adachokera ku South America makamaka dziko la Peru Ecuador ndi Mex...
31/05/2026

πŸ‡²πŸ‡Ό PHWETEKEERE AKUCHOKERA KU SOUTH AMERICA

Phwetekere adachokera ku South America makamaka dziko la Peru Ecuador ndi Mexico. Anthu a Aztec ndi Inca anali kulima ndi kudya kale zaka 500 BC ndipo dzina lakuti tomate linachokera ku chilankhulo cha Aztec chotchedwa Nahuatl.

Anthu aku Spain adabwera ndi phwetekere ku Europe mu 1500s atalanda ku Mexico. Koma poyamba anthu a ku Europe ankamuopa ndipo ankati ndi apulo wa poyizoni chifukwa anali kuona kuti ndi wachibale wa mbatata. Ankangolima ngati duwa lokongoletsa osadyedwa.

Phwetekere adapita ku Africa kudzera kwa amalonda a Chipwitikizi ndi Aarabu m'zaka za 1600s. Ku Malawi ndi madera ena a Southern Africa adafika mochedwa pafupifupi 1800s kudzera kwa amishonale ndi amalonda. Poyamba ankagwiritsidwa ntchito ngati mankhwala komanso zokongoletsa.

Kumapeto kwa 1700s ku Italy ndi Spain anthu adayamba kuphika ndi phwetekere. Ndipamene pizza spaghetti ndi msuzi wa phwetekere adabadwira. Ku Africa adatengedwa mwachangu chifukwa amamera mosavuta amabala kwambiri ndipo amapatsa thupi vitamini C ndi lycopene.

Lero phwetekere ndi imodzi mwa masamba ofunika kwambiri ku Malawi. Alimi ambiri ku Lilongwe Mchinji Dowa Thyolo ndi Mzimba amalima chifukwa amagulitsidwa chaka chonse. Amapezeka m'misika yonse m'masakana ngati pa chithunzi komanso m'masitolo. Amadyedwa yaiwisi yophika komanso amapangira msuzi ketchup ndi phala. Pali mitundu yoposa 10000 ya phwetekere padziko lonse lapansi ndipo mitundu yomwe imalimidwa kwambiri ku Malawi ndi Roma ndi Tengeru.

Phwetekere anayamba ngati duwa loopsya ku Europe lero ndi chakudya chomwe banja lililonse ku Malawi silingasiye.

Yalemekeza ndi: Mudzi Wathu News Online πŸ“°
WhatsApp link group MUDZI WATHU NEWS ONLINE πŸ“° https://chat.whatsapp.com/Ij7QmAC2u52LetKtEcdhMU
MUDZI WATHU NEWS ONLINE πŸ“° | NKHANI ZENIZENI, ZODALIRIKA .

πŸ‡²πŸ‡Ό  MADZI AUKHONDO AKUBWERA KU LILONGWE CITY BWAILA CONSTITUENCY VOTELANI DPP NDI MIKE CHIZUKILANgati muvotela DPP ndi M...
31/05/2026

πŸ‡²πŸ‡Ό MADZI AUKHONDO AKUBWERA KU LILONGWE CITY BWAILA CONSTITUENCY VOTELANI DPP NDI MIKE CHIZUKILA

Ngati muvotela DPP ndi Mike Chizukila pa 30 June 2026, madzi aukhondo adzafika mwachindunji m'midzi yonse ya Lilongwe City Bwaila Constituency.

Mike Chizukila ndi DPP pansi pa Professor Arthur Peter Mutharika alonjeza kuti ndalama za constituency development fund zidzagwira ntchito ku Lilongwe City Bwaila. Mu manifesto a DPP 2025-2030 anena momveka bwino kuti constituency iliyonse ilandira K5 billion pachaka. Ndalama izi zidzapita ku misewu, zaumoyo, sukulu ndi madzi aukhondo.

Ngati muvotela DPP ndi Mike Chizukila, ndalama za CDF zidzagwira ntchito kukumba zitsime zatsopano za madzi aukhondo ndi kuika mapampu a dzuwa m'midzi yonse ya Lilongwe City Bwaila. Zitsime zakale zowonongeka zidzakonzedwa nthawi yomweyo. Boma lidzayambanso kuika ma piped water system m'madera akumidzi kuti anthu asayende mtunda wautali.

Ngati muvotela DPP ndi Mike Chizukila ana anu ku Sukulu azizapita nthawi ya bwino chifukwa Madzi adidzapeza mosavuta kuti asambe, Matenda a m'mimba ngati kolera azichepa chifukwa banja lililonse lidzamwa madzi aukhondo. Mayi, mlimi ndi wamalonda aliyense ku Lilongwe City Bwaila azitha kutenga madzi pafupi ndi nyumba.

A Mike Chizukila ngati Phungu wachipani cholamula adzakambirana mwachindunji ndi boma kuti ndalama za CDF ndi mapulojekiti a madzi afike kwa anthu a Lilongwe City Bwaila mwachangu popanda kuchedwa.

DPP ikupempha anthu onse a Lilongwe City Bwaila Constituency. Ngati mukufuna madzi aukhondo, thanzi labwino ndi moyo wabwino, votelani DPP ndi Mike Chizukila pa 30 June 2026.

MUDZI WATHU NEWS ONLINE πŸ“° | NKHANI ZENIZENI, ZODALIRIKA.

πŸ‡²πŸ‡Ό  NDUNA YA DEFENCE OLEMEKEZEKA DR FESTON KAUPA APITA KU ZOMBA KUTHANDIZA MPINGONduna ya Defence olemekezeka Dr Feston ...
31/05/2026

πŸ‡²πŸ‡Ό NDUNA YA DEFENCE OLEMEKEZEKA DR FESTON KAUPA APITA KU ZOMBA KUTHANDIZA MPINGO

Nduna ya Defence olemekezeka Dr Feston Kaupa, M.P., Lamlungu adapita ku msonkhano wa Paper Sunday ku Parishi ya St Lawrence Kwipululu ku Boma la Zomba. Ndunayi yemwe ndi Mkristu wa Katolika adalowa nawo okhulupirika kuthandiza ndalama zomanga nyumba ya ansembe.

Misa yoyera idatsogoleredwa ndi Bishopu wa Dayosizi ya Zomba, Most Reverend Alfred Mateyu Chaima. Bishopu adalimbikitsa okhulupirika kuti azigwirizana ndi kupereka ndi mtima wogwirira ntchito za Mpingo.

Anthu mazana ambiri adapita ku msonkhanowu ndi mzimu wa umodzi komanso chikhulupiriro kuti athandize chitukuko cha Mpingo mderali.

Yalemekeza ndi: Mudzi Wathu News Online πŸ“°
MUDZI WATHU NEWS ONLINE πŸ“° | NKHANI ZENIZENI, ZODALIRIKA .

πŸ‡²πŸ‡Ό ANTHU AYAMIKIRA DEMOCRACY YA DPP PAMENE A VICTORIA KINGSTONE AKUWONEKA KU ZOCHITIKA ZA CHIPANICHI Anthu ochuluka tsop...
31/05/2026

πŸ‡²πŸ‡Ό ANTHU AYAMIKIRA DEMOCRACY YA DPP PAMENE A VICTORIA KINGSTONE AKUWONEKA KU ZOCHITIKA ZA CHIPANICHI

Anthu ochuluka tsopano ayamikira democracy imene ili mu chipani cha DPP. Izi zikudza kutsatila pomwe a Victoria Kingstone amene anali phungu wa dela la pakati pa Mangochi akumaoneka ku zochitika zambili za chipani cha DPP ngakhale kuti adagonja pa mpando wa phungu atapikisana kwambiri ndi a Roza Mbilidzi omwe pano ndi nduna ya zaulimi.

A Victoria Kingstone anali nawo pa nsonkhano wamakopedwe omwe unachitika ku Lilongwe ku dela la Bwaila komwe kuli zisankho zapadela pa 30 June 2026. Kukhalapo kwawo ku zochitika za DPP kukusonyeza kuti chipanichi ndi chotseguka ndipo chimakumbatira onse.

Ati izi zikungosonyeza kukula mu ndale kwa dziko lino. DPP ikutsimikiza kuti democracy yeniyeni ndi pamene anthu amagwirira ntchito limodzi pa chitukuko cha dziko.

Yalemekeza ndi: Mudzi Wathu News Online πŸ“°
MUDZI WATHU NEWS ONLINE πŸ“° | NKHANI ZENIZENI, ZODALIRIKA .

πŸ‡²πŸ‡Ό  AMA BUSINESS A BWAILA NDI MWAYI WANU KUDZERA MU THUMBA LA NGONGOLE LA DPPDPP yafotokoza ndondomeko yothandizira amal...
31/05/2026

πŸ‡²πŸ‡Ό AMA BUSINESS A BWAILA NDI MWAYI WANU KUDZERA MU THUMBA LA NGONGOLE LA DPP

DPP yafotokoza ndondomeko yothandizira amalonda ang'onoang'ono ku Bwaila Constituency. Zisankho za padela za Phungu wa nyumba ya malamulo zidzachitika pa 30 June 2026.

DPP yati ngati anthu avotela Mike Chizukila wa chipani cholamula, chitukuko chidzapita mwachindunji kwa amalonda. Iye ndi boma la DPP pansi pa Professor Arthur Peter Mutharika ayika thumba la ngongole pa constituency development fund. Thumba la ngongole limeneli ndi la amalonda ang'onoang'ono omwe amadalira malonda kuti adye.

Thumba la ngongole lidzathandiza amalonda kupeza ndalama zoyambira kapena kukulitsa bizinesi popanda zikalata zambiri. Mayi wogulitsa masamba, bambo wokonza nsapato, ndi mnyamata wogulitsa zinthu zazing'ono onse azitha kutenga ngongole yosavuta ndi yobwezera momasuka.

Kuphatikiza pa ngongole, DPP ilonjeza kuchepetsa misonkho ndi zilango zosafunika. Chipanichi chidzamanga malo ogulitsira aukhondo komanso otetezeka. Amalonda aphunzitsidwanso za kusunga ndalama ndi kukulitsa malonda kuti ngongole yomwe atenga iwachitire phindu.

A Mike Chizukila iye ngati Phungu wachipani cholamula adzakambirana mwachindunji ndi boma kuti thumba la ngongole ndi mapulogalamu ena afike kwa anthu a Bwaila popanda kuchedwa. Iye wapempha amalonda kuti asankhe chitukuko chowoneka.

DPP ikupempha amalonda onse a Bwaila kuti adzavote pa 30 June 2026. Voti yanu kwa Mike Chizukila ndi voti yachitukuko ndi moyo wabwino.

MUDZI WATHU NEWS ONLINE πŸ“° | NKHANI ZENIZENI, ZODALIRIKA .

πŸ‡²πŸ‡ΌπŸ‡«πŸ‡·πŸ‡¬πŸ‡§  PSG ILAMULIRA KU EUROPE ATAGONJETSA ARSENAL PA PENALTIESParis Saint-Germain yapambana mutu wa UEFA Champions Lea...
31/05/2026

πŸ‡²πŸ‡ΌπŸ‡«πŸ‡·πŸ‡¬πŸ‡§ PSG ILAMULIRA KU EUROPE ATAGONJETSA ARSENAL PA PENALTIES

Paris Saint-Germain yapambana mutu wa UEFA Champions League kachiwiri motsatizana atagonjetsa Arsenal ndi zigoli 4-3 pa ma penalty. Masewero omaliza adachitika tsiku la 31 May 2026 ku Budapest dziko la Hungary ndipo adatha 1-1 pambuyo pa mphindi 90 kuphatikiza extra time.

Kai Havertz adagoletsa goliyi yoyamba ya Arsenal, koma Ousmane Dembele adafanizira masewero ndi penalty mu gawo lachiwiri. Ma penalty shootout PSG idapambana pamene osewera a Arsenal Eberechi Eze ndi Gabriel Magalhaes adalephera kugoletsa. Achraf Hakimi ndiye adagoletsa penalty yomaliza yomwe idapatsa PSG mutuwo.

Kupambana kumeneku kwapangitsa PSG kukhala timu yachiwiri kuyambira 2018 kusunga Champions League motsatizana. Osewera a PSG adakweza chikho kutsogolo kwa mafani ambiri ku Puskas Arena.

Nkhani ina patsamba la masewero: Tabitha Chawinga wathandiza Lyon kupambananso ligi ya ku France kachiwiri, pomwe Timu ya Malawi Scorchers ikuyembekezeka kuyenda popanda Temwa Chawinga yemwe wapita ku China paulendo wa munthu payekha.

Yalemekeza ndi: Mudzi Wathu News Online πŸ“°
MUDZI WATHU NEWS ONLINE πŸ“° | NKHANI ZENIZENI, ZODALIRIKA .

πŸ‡­πŸ‡ΊπŸ‡«πŸ‡·πŸ‡¬πŸ‡§  PSG YAGONJETSA ARSENAL PA PENALTIES NDIKUTENGA CHAMPIONS LEAGUE 2026  nhttps://chat.whatsapp.com/Ij7QmAC2u52LetK...
30/05/2026

πŸ‡­πŸ‡ΊπŸ‡«πŸ‡·πŸ‡¬πŸ‡§ PSG YAGONJETSA ARSENAL PA PENALTIES NDIKUTENGA CHAMPIONS LEAGUE 2026

nhttps://chat.whatsapp.com/Ij7QmAC2u52LetKtEcdhMU

Masewero a UEFA Champions League final pakati pa Paris Saint-Germain ndi Arsenal adachitika tsiku la 30 May 2026 ku Puskas Arena ku Budapest dziko la Hungary.

Masewero adayamba mwamphamvu kwambiri. Pa miniti ya 6 wosewera wa Arsenal Kai Havertz adagoletsa goliyi yoyamba mothandizidwa ndi mpira woperekedwa bwino. Arsenal 1 PSG 0. Pambuyo pake PSG idayesa kwambiri kukwera ndi mpira koma chitetezo cha Arsenal chotsogoleredwa ndi Saliba ndi Gabriel chinali cholimba. Halftime idatha Arsenal 1 PSG 0.

Gawo lachiwiri PSG idabwerera ndi mphamvu zatsopano. Pa miniti ya 62 woweruza adapereka penalty ku PSG pambuyo poti wosewera wa Arsenal Cristhian Mosquera adagwetsa Khvicha Kvaratskhelia mdera la penalty. Ousmane Dembele adagoletsa penaltyyo pa miniti ya 65 ndipo masewero anafanana 1-1.

Mphindi 90 zidadutsa palibe timu yomwe idakwera. Woweruza adawonjezera extra time ya mphindi 30 koma palibe goliyo ina idalowa. Masewero anamaliza 1-1 ndipo adayenera kuthetsedwa ndi ma penalty.

Ma penalty shootout anali ovuta. Arsenal idayamba kugoletsa koma PSG idayankha. Pamapeto pake PSG idapambana ndi zigoli 4-3 pa penalties. Donnarumma adachita save imodzi yofunika kwambiri yomwe idapangitsa PSG kupambana.

Chifukwa cha kupambana kumeneku PSG yakhala timu yoyamba kuyambira Real Madrid ya 2018 kusunga Champions League motsatizana. Luis Enrique ndi osewera ake adalemba mbiri ku Europe.

Yalemekeza ndi: Mudzi Wathu News Online Huawei pa internet πŸ“°
MUDZI WATHU NEWS ONLINE πŸ“° | NKHANI ZENIZENI, ZODALIRIKA .

πŸ‡²πŸ‡Ό BWAILA WASANKHA CHITUKUKO CHACHANGU NDI MIKE CHIZUKILA WA DPPLilongwe β€” Anthu a Lilongwe City Bwaila Constituency ati...
30/05/2026

πŸ‡²πŸ‡Ό BWAILA WASANKHA CHITUKUKO CHACHANGU NDI MIKE CHIZUKILA WA DPP

Lilongwe β€” Anthu a Lilongwe City Bwaila Constituency ati pa 30 June 2026 sadzalakwitsa. Iwo agwirizana kuti Mike Chizukila wa Democratic Progressive Party DPP ndiye phungu woyenera kumupatsa voti yawo.

Chifukwa chawo ndi chosavuta. Chipani cholamula chili ndi mphamvu zofikira ku boma mwachindunji. Izi zikutanthauza kuti ngati pali vuto la misewu, sukulu kapena zipatala ku Bwaila, phungu wa DPP azilankhula ndi nduna mwachangu ndipo yankho lidzafika popanda kuchedwa.

Mu manifesto ya DPP muli zolinga zomveka. Maphunziro abwino kwa ana onse, zipatala zodzaza ndi mankhwala, achinyamata alandire luso ndi ndalama zoyambira mabizinesi, komanso chakudya chokwanira m’banja lililonse. Anthu a Bwaila ati izi ndi zomwe akufuna lero, osati malonjezo a mawa.

Kuphatikiza apo, utsogoleri wa Professor Arthur Peter Mutharika ndi chitsanzo kwa iwo. Nthawi yake dziko la Malawi lidawona misewu yatsopano, magetsi kufika kumadera ambiri, ndiponso ulimi kulimbikitsidwa. Mike Chizukila akulonjeza kugwira ntchito pansi pa masomphenya amenewo kuti Bwaila isinthe.

Choncho mawu a Bwaila ndi amodzi: pa 30 June 2026 tivote Mike Chizukila wa DPP. Voti yathu ndi ya chitukuko chomwe chikufika mbali zonse mwachangu.

MUDZI WATHU NEWS ONLINE πŸ“° | NKHANI ZENIZENI, ZODALIRIKA

Address

Msanje Mpaka Chitipa
Lilongwe
MUDZIWATHUNEWSONLINE

Website

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Mudzi wathu news online : Nkhani Zenizeni, zodalirika posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Share