Radio Maria Malawi

Radio Maria Malawi RADIO MARIA is a broadcasting initiative, which was started in Italy by a group of Catholics, both priests and lay people. The radio is not commercially funded.

It aims at spreading the Good News of Jesus Christ to all people of good will.

Episikopi wothandizira mu Arkidayosizi ya Lilongwe, Ambuye Vincent Mwakhwawa walangiza akhrisitu omwe alandira sakrament...
26/08/2026

Episikopi wothandizira mu Arkidayosizi ya Lilongwe, Ambuye Vincent Mwakhwawa walangiza akhrisitu omwe alandira sakramenti la Ulimbitso ku parishi ya St. Patrick's Area 18 kuti akuyenera kukhazikika m'moyo wokonda mapemphero komanso kudziletsa ku zochitika zomwe zingasokoneze chikhristu chawo.

Ambuye Mwakhwawa ati kulandira sakramenti la Ulimbitso si mathero a ulendo mu utumiki kwa achinyamata koma chiyambi cha kusinkhasinkha mozama zokhudza mayitanidwe osiyanasiyana.

Iwo adandaulaso kuti maparishi a m'matawuni sakhala ndi chidwi cholimbikitsa achinyamata kulowa unsembe kapena usisteri zomwe zakhala zikuchepetsa chiwerengero cha atumiki mu mpingo wa Katolika choncho apempha makolo kuti adzipereka mpata kwa ana awo kusankha mautumiki osiyanasiyana ndi cholinga chopititsa mpingo patsogolo.

Achinyamata 82 ndi omwe alandira sakramenti la Ulimbitso ku parishi ya St. Patrick's Area 18 mu Arkidayosizi ya Lilongwe.

Mkulu woyendetsa ntchito za sukulu za Maranatha, Dr. Ernest Kaonga wati ayimitsa ena mwa omwe amagwira ntchito yosankha ...
26/08/2026

Mkulu woyendetsa ntchito za sukulu za Maranatha, Dr. Ernest Kaonga wati ayimitsa ena mwa omwe amagwira ntchito yosankha ana omwe akuyembekezeka kusankhidwa kuti akhale nawo mu gulu la ana opindula pophunzira mwaulere m'sukulu za Maranatha, kaamba koti akukayikiridwa kuti amachita zachinyengo kuti akondere ana ena powasankha kuti achita bwino.

De. Kaonga ayankhula izi mu mzinda wa Blantyre pa mkumano wa atolankhani omwe anachititsa ndi cholinga chofuna kufotokozera m'mene ndondomeko yosankha anawa ikuyendera kutsatira mayeso omwe analembetsa mzigawo zonse za dziko lino.

Pamenepa iwo ati ana omwe analemba mayesowa asadere nkhawa kaamba koti awonetsetsa kuti pasachitike zachinyengo pa mndandanda wa ana omwe apeze mwayi wokaphunzira m'sukulu za Maranatha mwaulere.

Ana omwe akuyembekezeka kupeza mwayi wokaphunzira m'sukulu za Maranatha mwaulere ndi okwana 500.

Bungwe lotolera msonkho mdziko muno la Malawi Revenue Authority (MRA) lakhazikitsa ndondomeko yake ya zochitika (Corpora...
24/08/2026

Bungwe lotolera msonkho mdziko muno la Malawi Revenue Authority (MRA) lakhazikitsa ndondomeko yake ya zochitika (Corporate Strategic Plan) ya mchaka cha 2026 mpaka 2031.

Ndondomekoyi yakhazikitsidwa pa mutu woti; Leveraging Digital Transformation for Sustained Revenue Growth and Efficient Service.

Poyankhula pa mwambo wokhazikitsa ndondomekoyi mu mzinda wa Blantyre, nduna ya zachuma, mapulani ndi chitukuko, a Joseph Mwanamveka ati ndi okhutira ndi momwe bungweli likugwilira ntchito zake potengera kuti likutha kukwaniritsa ndi kupyola mulingo wa ndalama zomwe amapatsidwa kuti atolere.

Pamenepa ndunayi yati ili ndi chikhulupiliro kuti ndondomeko zomwe bungweli lakhazikitsa lichita bwino.

Mwapadera a Mwanamveka ayamikira anthu omwe amadula msonkho kaamba komvetsetsa ndi kuyamba kukhulupirika pa ndondomeko ya makono yolondoloza msonkho kuti ukuperekedwa moyenera ya Electronic Invoicing System (EIS)

24/08/2026
24/08/2026

Mwambo wa msembe ya Ukaristia wokondwelera zaka 27 za Radio Maria Malawi

Akhristu aku parishi ya Namandanje mu Dayosizi ya Mangochi,  apereka njinga yamoto yatsopano kwa wansembe watsopano woch...
23/08/2026

Akhristu aku parishi ya Namandanje mu Dayosizi ya Mangochi, apereka njinga yamoto yatsopano kwa wansembe watsopano wochokera ku parishiyo, Bambo Alfred Semani Banda, pamene akuyamba utumiki wake.

Njingayi yaperekedwa lero pa Misa yomwe inachitika ku tchalitchi la St. Anna lomwe ndi nthambi ya parishiyo komwe ndi kwawo kwa bambowa.

Vicar General wa Dayosizi ya Mangochi, Bambo Davie Mambo, omwe anatsogolera mwambowu, ayamikira akhristu aku parishiyo kaamba kopereka mphatsoyi komanso popereka chitsanzo chabwino kwa akhristu a maparishi ena.

Bambo Banda ati njingayi iwathandiza kutumikira mosavuta ku madera akutali komwe kwina mwa iko ndi kovuta mayendedwe.

Yemwe akugwirizira udindo wa mkulu woyendetsa ntchito za banki ya Centenary m'dziko muno, mayi Beatrix Mosiwa watsutsa m...
23/08/2026

Yemwe akugwirizira udindo wa mkulu woyendetsa ntchito za banki ya Centenary m'dziko muno, mayi Beatrix Mosiwa watsutsa mphekesera zomwe zakhala zikuzungulira m'masamba a mchezo a pa intaneti kuti bankiyi siyinapeze phindu lililonse kuchokera pomwe inayamba.

Iwo ati ili ndi bodza ndipo posachedwapa afotokozera Amalawi momwe bankiyi yachitira m'chaka cha 2025.

Poyankhulapo mlangizi wa bankiyi
Bambo John Mangwele ati ntchito za bankiyi zikuyenda bwino ndipo posachedwa akhala akutsekula nthambi zina ziwiri m'maboma a Karonga ndi Salima chaka chino chisanathe.

Banki ya Centenary yomwe ndi ya Arkidayosizi ya mpingo wa Katolika ya Lilongwe, idayamba kugwira ntchito zake m'chaka cha 2023, ndipo padakali pano ili ndi nthambi zokwana 16 m'madera osiyanasiyana m'dziko muno.

Episkopi wa dayosizi ya Mangochi, Ambuye Montfort Stima, wati ndi kofunika kuti akhristu achulukitse mapemphero ndi kuti...
23/08/2026

Episkopi wa dayosizi ya Mangochi, Ambuye Montfort Stima, wati ndi kofunika kuti akhristu achulukitse mapemphero ndi kuti amvetse bwino cholinga cha chibalalitso cha mpingo.

Iwo ayankhula izi lero ku parishi ya St. Martin de Pores Nsanama mu dayosiziyo pamene anatsogolera Misa yokhazikitsa zokonzekera za chibalalitso cha mpingo cha chaka chino mu dayosiziyo, chomwe chidzachitike pa 18 October 2026.

Iwo ati kumvetsa bwino za chibalalitso kuthandiza kuti akhristu apereke moolowa manja pa ntchito yobalalitsa mpingo kudzera mu kumanga matchalitchi, nyumba za ansembe, sukulu, ndi zinthu zina zofunikira kuti uthenga wa Mulungu ufalikire mosavuta.

Poyankhulapo moderator wa parishi ya Nsanama, a Harlod Sitima ati parishi yawo ndi yokozeka kutsogolera chibalalitso cha chaka chino mu dayosiziyo ndipo ayika ndondomeko zabwino zowathandiza kutolera ndalama zokwanira za chibalalitso.

Chibalalitso cha mpingo chaka chino chikukondweleredwa pa mutu woti; "Kukhala amodzi mwa Khristu, kugwirizana pa utumiki."

M'modzi mwa ansembe opuma mu Arkidayosizi ya Lilongwe, Bambo Alufeyo Zikomankhani ayamikira ogwira ntchito ku banki ya C...
23/08/2026

M'modzi mwa ansembe opuma mu Arkidayosizi ya Lilongwe, Bambo Alufeyo Zikomankhani ayamikira ogwira ntchito ku banki ya Centenary kaamba kowachezera ndi kuwapatsa katundu wosiyanasiyana.

Iwo ayankhula izi kunyumba ya ansembe opuma mu Arkidayosizi ya Lilongwe yomwe ikupezeka ku Likuni, pamene gulu la ogwira ntchito ku bankiyi linawabweretsera katundu wosiyanasiyana wa ndalama zoposa 1 million kwacha.

Poyankhulapo mlangizi wa banki ya Centenary, Bambo John Mangwele, ati kunali kofunika kuyendera ndi kulimbikitsa atumiki opumawa pokumbukira ntchito zawo zabwino zomwe anagwira potumika mpingo.

Bambo Audifansio Kapinga komanso Bambo Anselmo Chiwaya, ndi ena mwa ansembe opuma omwe amakhala ku nyumbayi.

Address

Box 408, Mangochi
Chimwala

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Radio Maria Malawi posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Organization

Send a message to Radio Maria Malawi:

Shortcuts

Share