HON ENOCK Chizuzu, Nsanje North Sons & daughters

HON ENOCK Chizuzu, Nsanje North Sons & daughters Contact information, map and directions, contact form, opening hours, services, ratings, photos, videos and announcements from HON ENOCK Chizuzu, Nsanje North Sons & daughters, Community Organization, nsanje, Nsanje.

Enock Masautso Chizuzu Was a dedicated law maker in Nsanje North constituency, he comes from the clan of Mbuya Gwanda Chakuamba and won in 2020 parliamentaryelections under MCP Ticket.

09/09/2025

MNSONKHANO WOYIMAYIMA

Mmawa pa 10th September 2025, lomwe ndi lachitatu. A President Dr Lazarus Chakwera akhale ndi mnsonkhano woyendera anthu ku Nsanje North ( whistle Stop Tour)

A President Chakwera azakhale akuima pa Chinyanje Trading Centre kenako azakafika pa Fatima Boys, tiyeni tonse tizakhamukire mmadera tatchulawa ndikuzamvera mfundo za Chitukuko.

Achinyamata, azimayi, azibambo nthawi yakwana taono imene Tate wafuko akufuna kuzacheza nanu. Ndipotu game iyiyi, ndi Wadya Mtoliro.

Vote for Enock Chizuzu MP, vote for Dr Lazarus McCarthy Chakwera- President of the Republic of Malawi

OSIYANA RALLYKunali khwimbi la anthu kwa Osiyana pa 3 September 2025 pamene ndimacheza ndi abale ndi alongo pa ulendo wo...
04/09/2025

OSIYANA RALLY

Kunali khwimbi la anthu kwa Osiyana pa 3 September 2025 pamene ndimacheza ndi abale ndi alongo pa ulendo wopita ku Chisankho cha pa 16 September 2025.

Tithokoze mafumu, ndi akulu akulu ena amene anatsogolera mwambo olandira anthu oposa 100 ochoka kuchipani cha DPP. Anthuwa lero alowa chipani chokondedwa cha MCP ndipo avomereza zozavotera Dr Lazarus Chakwera

Mwa mfundo zina.Kwa Osiyana ndidaunikira za zitukuko zosiyana siyana zomwe tachita monga kukonzaso magetsi a pachipatalachi, kubweretsa madzi komanso kuonetsetsa mayendedwe a magalimoto ndi ofikirika kupita ku chipatalachi.

Izi ndizochepa chabe zochokera kwa Osiyana koma tikuyenda ndithu ndipo tifotokozaso mmene tidayendera ku M'bwazi ndi Namilembe

-Enock-Chizuzu

03/09/2025

ZITUKUKO IZI ZILI PATI?

Lero pa 3 September 2025 tiyeni tikhamukire ku Namilembe ground kumene mwana wa mudzi, Hon Enock chizuzu chizuzu akhale akhale akukonzekera komanso kuyankha mafunso okhudza zazitukuko ku Nsanje North.

Kodi chiliza cha Gwanda Chakuamba zili pati?

Yankho lake ndi la straight Forward, za Chiliza cha Mbuya Chakuamba zinachedwa chifukwa cha zokambilana pakati pa akubanja ndi boma posintha design ya Chiliza mmene Chikhalire. Mbali ziwirizi zitamaliza kukambilana, ine monga Mphungu ndidabweretsa Contractor kupanga handover kuti amange Chilizachi. Mmene zinatere ndekuti mbali yanga ndidachita idatsala mbali ya contractor komanso akubanja kutsatira za kamangidwe ka malo ogona a Mbuya Chakuamba.

Funso lina, Kodi za Maref zili pati?
Yankho lake lili motere. Nditamaliza kubweretsa transformer kwa Chambuluka kudzera kwa a pulezidenti a Chakwera ine monga Phungu ndidaonetsetsa kuti boma libweretse magetsi kwa Alufazema, Mpembamoyo, Osiyana komanso Mchacha Jemusi ndipo kunatsala ndi kuyatsa basi. Kotero mbali yanga chitukuko cha magetsi chinafika.

Funso lina mkumati, Kodi za Makhapa Scheme zili pati?
Yankho lake nali. Zakuti Makhapha Scheme inapangidwa komanso idayamba kugwira ntchito tonse tikudziwa. Pokha pokha kwa iye amene amakhala mtauni kapena wabwera kumene ku Nsanje North sangazitsate. Makhapha Scheme inayamba kugwira bwino ntchito koma vuto anthu awupandu mudabwera kuzaba ma solar onse ndi pump cholinga mubwezeretsa chitukuko m'mbuyo. Chitukuko chikabwera pamalo zimagunika mafumu anthu a mmudzi kuchilimika kusamalira zithu, a Pulezidenti kapena mphungu sangapezeke paliponse kukhala olondera zitukuko. Chonde tiyeni tizisamalira zitukuko

Funso lina lokhudza Muona Scheme.
Uku oyendera anabwera kale kudzayendera ndipo kwatsala ndikoti kubwere contractor ayambe ntchito.

Zikomo
-Enock-Chizuzu

MSONKHANO WAUKULU OTAMBASULA MANIFESTO A DR LAZARUS CHAKWERA Tiyeni tonse tipite pa Namilembe Primary school lachitatu l...
01/09/2025

MSONKHANO WAUKULU OTAMBASULA MANIFESTO A DR LAZARUS CHAKWERA

Tiyeni tonse tipite pa Namilembe Primary school lachitatu likubwerali, uku mkumene Hon Chizuzu akakhale ndi mnsonkhano waukulu ocheza ndi anthu ochita ma Business, achinyamata komanso azimayi.

Lachitatu likubwerali pa 3 September 2025 a vice president a Chipani cha MCP, Hon Abida Mia akhale akutambasula Manifesto a Chipani Chipani chathu chokondedwa cha MCP.

Tikutitu azimayi ndi azibambo tiyeni tonse ku Namilembe Primary school takamve mfundo zotchakuka

-Chizuzu-MP

MSONKHANO WA KWA OSIYANA.Pa nthawi ino yakuchita campaign kuno ku Nsanje North pamene tikukonzekera zisankho za patatu (...
28/08/2025

MSONKHANO WA KWA OSIYANA.

Pa nthawi ino yakuchita campaign kuno ku Nsanje North pamene tikukonzekera zisankho za patatu (tripartite elections) ndidapita kwa Osiyana kumene unyinji wa munthu unandilandira ndikunditsimikizira kuti iwo ali okonzeka kuvoteraso ine monga mphungu wawo pa 16 September 2025 komanso kuvotera Dr Lazarus Chakwera kuti tipitirize zitukuko zimene takhala tikuchilimika.

Apa Zatsimikizika kuti abale ambiri ku Nsanje North ali mtika mweni mweni mwa Boma la MCP, ndipo cholinga chawo ndikuvotera MCP basi.

_ kumada ndipo kumacha

-Enock-Chizuzu

NSANJE NORTH MEGA RALLYKuli Mkokekoke pa Fatima Ground kumene 2nd Vice president wa Chipani cha MCP Olemekezeka a Abida ...
16/08/2025

NSANJE NORTH MEGA RALLY

Kuli Mkokekoke pa Fatima Ground kumene 2nd Vice president wa Chipani cha MCP Olemekezeka a Abida Mia akhale akutsogolera chi mnsonkhano chachikulu kumene akakhale akutambasula manifesto a 2025.

Olemekezeka Abida Mia aperekezedwa ndi Hon Peter Simbi, Hon Kafa Ndikhale Mandevana, Hon Dc Peter Kamanga, Hon Seluby Chisanga, Hon Florence Nanyoni komanso Hon Bernadette Mlaka Maliro.

Tiyeni tonse tikhamukire pa Fatima Ground kumene kukhale mfundo za Chitukuko

-Enock-Chizuzu

Pictorial focus, Opening of Muona Police unit
02/08/2025

Pictorial focus,

Opening of Muona Police unit

01/08/2025

KUTSEGULIRA MUONA POLICE UNIT.

Kwa Nthawi yayitali kwa T/A Mlolo kwakhala kuli police unit imodzi yodalilika kwambiri ya pa Fatima. Ngakhale kuti kuliso ma police unit ena ang'onoang'ono koma milandu yambiri imathera pa Fatima Trinity.

Koma lero ndili okondwa pamene Boma latipatsa Police Unit ya Muona imene yamangidwa mochititsa kaso ndipo ikhale ikuthandizira kuthetsa ntchito za umbanda ku Nsanje North.

M***a kutsimikiza inu kuti zitukukozi zabwera mwa kathithi pa zaka zimene ndakala ndikutumikira pansi pa Dr Lazarus Chakwera mu chipani cha MCP. Apa ndiye olo tikamati boma ndilomweri sitingalakwitse pakuti ine monga Phungu wanu kundipatsaso zaka zina zisanu ndi a Chakwera tizaonetsetsa kuti zitukuko zifikire ponse ponse

Hon Enock Chizuzu

KUNJA KUMADA NDIPO KUMACHALero pa 27 July 2025 ine monga mphungu wa ku Nsanje North ndikhale ndikukapereka mapepala pa F...
27/07/2025

KUNJA KUMADA NDIPO KUMACHA

Lero pa 27 July 2025 ine monga mphungu wa ku Nsanje North ndikhale ndikukapereka mapepala pa Fatima Teacher’s Development Centre ,ndikapereka mapepalawa ndikhala ndatsimikiza kuti ndizayimilaso pa 16 September mu zisankho zapatatu.

Ndikatero ndikumema onse ondisapota kuti tikasonkhane pa Fatima Boys ground kumene ndikukakhazikitsa ulendo ochita campaign.

Ulendo uno kukhale kuthamanga osati chibwana (leaving no stone un turned) tiyeni tonse tivale makaka a chipani chathu cha MCP, amene tilibe bwerani ndipo nsalu zikapezeka komweko.

Tikatero timati
Kwacha!

-Enock-Chizuzu

BENEFICIARIES OF CDF BURSARY.Ndili okondwa pofuna kukudziwitsani kuti lero pa 15 July 2025 ndakwanitsa kulipirira ophunz...
15/07/2025

BENEFICIARIES OF CDF BURSARY.

Ndili okondwa pofuna kukudziwitsani kuti lero pa 15 July 2025 ndakwanitsa kulipirira ophunzira oposa amene ali pa Constituency development fund bursary

Ophunzirawa akuphunzira masukulu osiyanasiyana monga

1- Nsanje Sec Sch
2- Bangula Sec Sch
3- Namilembe CDSS
4- Makhanga CDSS
5- Fatima CDSS
6- Masenjere CDSS

-Chizuzu-MP

Madzulo abwino abale ndi alongo.Lero pa 14 July 2025 bungwe loyendetsa zisankho la Malawi Electoral Commission yatseguli...
14/07/2025

Madzulo abwino abale ndi alongo.
Lero pa 14 July 2025 bungwe loyendetsa zisankho la Malawi Electoral Commission yatsegulira campaign pokonzekera zisankho za patatu (tripartite elections) zomwe zichitike pa 16 September 2025.

Ine monga Mphungu wanu ku Nsanje North ndili okonzeka kupanga campaign ya bata komanso yololerana. Chomwechonse ndikumema anzanga onse a zipani zosiyanasiyana siyana kupanga campaign ya mfundo za chitukuko, kupewa kunyoza ndi kutukwanizana. Achinyamata komanso azimayi tisalore kugwiritsidwa ntchito ndi a ndale.

Tiyeni timange Malawi wa Chitukuko.

-Enock-Chizuzu

Address

Nsanje
Nsanje
265

Website

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when HON ENOCK Chizuzu, Nsanje North Sons & daughters posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Organization

Send a message to HON ENOCK Chizuzu, Nsanje North Sons & daughters:

Share